< 1 Kings 16 >
1 Then came the word of the Lord to Jehu the son of Chanani against Ba'sha, saying,
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 Forasmuch as I lifted thee up out of the dust, and I set thee as prince over my people Israel; and thou hast walked in the way of Jerobo'am, and hast induced my people Israel to sin, to provoke me to anger with their sins:
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Behold, I will sweep out after Ba'sha, and after his house; and I will render thy house like the house of Jerobo'am the son of Nebat;
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Him that dieth of Ba'sha in the city shall the dogs eat; and him that dieth of his in the field shall the fowls of the heavens eat.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 And the rest of the acts of Ba'sha, and what he did, and his mighty deeds, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 And Ba'sha slept with his fathers, and was buried in Thirzah: and Elah his son became king in his stead.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 And also by the hand of Jehu the son of Chanani, the prophet, came the word of the Lord against Ba'sha, and against his house, both for all the evil that he did in the eyes of the Lord, to provoke him to anger with the work of his hands, thus being like the house of Jerobo'am; and because he had killed him.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 In the twenty and sixth year of Assa the king of Judah became Elah the son of Ba'sha king over Israel in Thirzah, [for] two years.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 And there conspired against him his servant Zimri, captain of half the chariots, as he was in Thirzah, drinking himself drunk in the house of Arza, who was set over the house in Thirzah.
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 And Zimri went in and smote him, and killed him, in the twenty and seventh year of Assa the king of Judah, and became king in his stead.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 And it came to pass, when he began to reign, as soon as he sat on his throne, that he slew all the house of Ba'sha: he left him not a single male, neither of his kinsfolks, nor of his friends.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Thus did Zimri exterminate all the house of Ba'sha, according to the word of the Lord, which he had spoken against Ba'sha by the agency of Jehu the prophet,
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 For all the sins of Ba'sha, and the sins of Elah his son, by which they had sinned, and by which they had induced Israel to sin, to provoke the Lord the God of Israel to anger with their vanities.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Now the rest of the acts of Elah, and all that he did, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 In the twenty and seventh year of Assa the king of Judah did Zimri reign seven days in Thirzah: and the people were encamped against Gibbethon, which belonged to the Philistines.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 And when the people that were encamped heard it said, Zimri hath conspired, and hath also slain the king: all Israel made 'Omri, the captain of the army, king over Israel on that day in the camp.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 And 'Omri went up, and all Israel with him from Gibbethon, and they besieged Thirzah.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 And it came to pass, when Zimri saw that the city was captured, that he went into the strong-hold of the king's house, and burnt the king's house over him with fire, and he died;
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 For his sins which he had sinned, in doing what is evil in the eyes of the Lord, to walk in the way of Jerobo'am, and in his sin which he did, to induce Israel to sin.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 And the rest of the acts of Zimri, and his conspiracy that he contrived, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 At that time were the people of Israel divided into two parts: one half of the people followed Thibni the son of Ginath, to make him king; and the other half followed 'Omri.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 But the people that followed 'Omri prevailed against the people that followed Thibni the son of Ginath: and Thibni [also] died, and 'Omri became king.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 In the thirty and first year of Assa the king of Judah became 'Omri king over Israel, [for] twelve years; in Thirzah he reigned six years.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 And he bought the mount Samaria, of Shemer for two talents of silver, and built on the mount, and called the name of the city which he had built, after the name of Shemer, the Lord of the mount, Samaria.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 And 'Omri did what is evil in the eyes of the Lord, and did worse than all that were before him.
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 And he walked in all the way of Jerobo'am the son of Nebat, and in his sin wherewith he induced Israel to sin, to provoke the Lord God of Israel to anger with their vanities.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Now the rest of the acts of 'Omri which he did, and his mighty deeds that he displayed, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 And 'Omri slept with his fathers, and was buried in Samaria: and Achab his son became king in his stead.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 And Achab the son of 'omri became king over Israel in the thirty and eighth year of Assa the king of Judah; and Achab the son of 'Omri reigned over Israel in Samaria twenty and two years.
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 And Achab the son of 'Omri did what is evil in the eyes of the Lord more than all that had been before him.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 And it came to pass, as if it had been too light a thing for him to walk in the sins of Jerobo'am the son of Nebat, that he took for wife Izebel the daughter of Ethba'al the king of the Zidonians, and went and served Ba'al, and worshipped him.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 And he erected an altar for Ba'al in the house of Ba'al, which he had built in Samaria.
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 And Achab made a grove; and Achab did yet more, so as to provoke the Lord the God of Israel to anger, than all the kings of Israel that had been before him.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 In his days did Chiel the Beth-elite build Jericho: with Abiram his first-born laid he the foundation thereof, and with Segub his youngest son set he up the gates thereof, according to the word of the Lord, which he had spoken by means of Joshua the son of Nun.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.