< 1 Kings 13 >

1 And, behold, there came a man of God out of Judah by the word of the Lord unto Beth-el: while Jerobo'am was standing upon the altar to burn incense.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 And he called out against the altar by the word of the Lord, and he said, O altar, altar, thus hath said the Lord, Behold, a child shall be born unto the house of David, Josiah by name, and he shall sacrifice upon thee the priests of the high-places that burn incense upon thee, and men's bones shall be burnt upon thee.
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 And he gave on the same day a token, saying, This is the token that the Lord hath spoken, Behold, the altar shall be rent, and the ashes which are upon it shall be spilled about.
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 And it came to pass, when the king heard the word of the man of God, which he had called out against the altar in Beth-el, that Jerobo'am stretched forth his hand from off the altar, saying, Seize him. And his hand, which he had put forth against him, dried up, so that he could not draw it back to himself.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 The altar also was rent, and the ashes were spilled about from the altar, according to the token which the man of God had given by the word of the Lord.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 And the king commenced and said unto the man of God, Offer but entreaty before the Lord thy God, and pray in behalf of me, that my hand may return to me again. And the man of God offered his entreaty before the Lord, and the king's hand returned to him again, and became as it was before.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 And the king spoke unto the man of God, Come home with me, and take some refreshment, and I will give thee a present.
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 But the man of God said unto the king, If thou wert to give me the half of thy house, I would not go in with thee, neither would I eat bread nor drink water in this place;
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 For so was it charged me by the word of the Lord, saying, Thou shalt not eat bread, nor drink water, nor return by the way that thou camest.
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 So he went by another way, and returned not by the way on which he was come to Beth-el.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 Now there dwelt a certain old prophet in Beth-el; and his son came and told him all the deed that the man of God had done that day in Beth-el: the words [also] which he had spoken unto the king, these too they told to their father.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 And their father spoke unto them, What way did he go? His sons however had seen what way had gone the man of God, who had come from Judah.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 And he said unto his sons, Saddle me the ass. So they saddled him the ass, and he rode away thereon,
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 And he went after the man of God, and found him sitting under the oak; and he said unto him, Art thou the man of God that camest from Judah? And he said, I am.
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 Then said he unto him, Come with me home, and eat bread.
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 And he said, I cannot return with thee, nor go in with thee: neither will I eat bread nor drink water with thee in this place;
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 For a command came to me by the word of the Lord, Thou shalt not eat bread nor drink water there; thou shalt not return to go by the way [also] by which thou camest.
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 And he said unto him, I also am a prophet like thee; and an angel spoke unto me by the word of the Lord, saying, Bring him back with thee unto thy house, that he may eat bread and drink water. But he lied unto him.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 So he returned with him, and ate bread in his house, and drank water.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 And it came to pass, as they were sitting at the table, That the word of the Lord came unto the prophet who had brought him back;
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 And he called unto the man of God that was come from Judah, saying, Thus hath said the Lord, Forasmuch as thou hast disobeyed the order of the Lord, and hast not kept the commandment which the Lord thy God had commanded thee;
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 But didst return, and hast eaten bread and drunk water in the place, of which he had spoken to thee, Thou shalt not eat bread, nor drink water: thy dead body shall not come unto the sepulchre of thy fathers.
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 And it came to pass, after he had eaten bread, and after he had drunk, that he saddled for him the ass, [to wit, ] for the prophet whom he had brought back.
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 And when he was gone, a lion met him on the way, and slew him; and his corpse remained cast down on the way, and the ass stood by it, the lion also stood by the corpse.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 And, behold, men passed by, and saw the corpse cast down on the way, and the lion standing by the corpse; and they came and spoke of it in the city where the old prophet dwelt.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 And when the prophet that had brought him back from the way heard it, he said, It is the man of God who was disobedient unto the order of the Lord; wherefore the Lord hath given him up unto the lion, who hath torn him, and slain him, according to the word of the Lord, which he had spoken unto him.
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 And he spoke to his sons, saying, Saddle me the ass. And they saddled him.
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 And he went and found his corpse cast down on the way, and the ass and the lion standing by the corpse: the lion had not eaten the corpse, nor torn the ass.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 And the prophet took up the corpse of the man of God, and laid it upon the ass, and brought it back; and he came to the city of the old prophet, to lament for, and to bury him.
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 And he laid his corpse in his own sepulchre; and they lamented over him, “Alas, my brother!”
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 And it came to pass, after he had buried him, that he spoke to his sons, saying, When I am dead, then bury me in the sepulchre wherein the man of God is buried; beside his bones lay ye my bones;
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 For the thing which he called out by the word of the Lord against the altar which is in Beth-el, and against all the houses of the high-places which are in the cities of Samaria, will surely come to pass.
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 After this event Jerobo'am returned not from his evil way; but made again of the lowest of the people priests of the high-places: whosoever desired it, he consecrated, that he might become one of the priests of the high-places.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 And he became through this thing the cause of sin unto the house of Jerobo'am, and to cause that it was blotted out, and destroyed from off the face of the earth.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Kings 13 >