< 1 Chronicles 7 >

1 And the sons of Issachar were, Tola', and Puah, Yashub, and Shimron, four.
Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
2 And the sons of Tola': 'Uzzi, and Rephayah, and Jeriel, and Jachmai, and Yibsam, and Shemuel, heads of their family divisions, of Tola', being valiant men of might, after their descent. Their number in the days of David was two and twenty thousand and six hundred.
Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
3 And the sons of 'Uzzi: Yizrachyah. And the sons of Yizrachyah: Michael, and 'Obadiah, and Joel, Yishiyah, five, chief men all of them.
Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
4 And with them according to their descent, after their family divisions, were bands of the army for war, six and thirty thousand men; for they had many wives and sons.
Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
5 And their brethren of all the families of Issachar were valiant men of might, eighty and seven thousand reckoned by their genealogies in all.
Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
6 Of Benjamin: Bela', and Becher, and Jedi'ael, three.
Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
7 And the sons of Bela': Ezbon, and 'Uzzi, and 'Uzziel, and Jerimoth, and 'Iri, five, heads of family divisions, being mighty men of valor; and they were reckoned by their genealogies twenty and two thousand and thirty and four.
Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
8 And the sons of Becher: Zemirah, and Jo'ash, and Eli'ezer, and Elyo'enai, and 'Omri, and Jeremoth, and Abiyah, and 'Anathoth, and 'Alemeth. All these are the sons of Becher.
Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
9 And reckoned by their genealogy after their descent, heads of their family divisions, mighty men of valor, there were twenty thousand and two hundred.
Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
10 And the sons of Jedi'ael: Bilhan. And the sons of Bilhan: Je'ush, and Benjamin, and Ehud, and Kena'anah, and Zethan, and Tharshish, and Achishachar.
Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
11 All these the sons of Jedi'ael by the heads of their divisions, being mighty men of valor, were seventeen thousand and two hundred, fit to go out to the army for war.
Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
12 And Shuppim, and Chuppim, the children of 'Ir, and Chushim, the sons of Acher.
Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
13 The sons of Naphtali: Jachziel, and Guni, and Jezer, and Shallum, the sons of Bilhah.
Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
14 The sons of Menasseh: Assriel, whom [his wife] bore; his concubine the Aramitess bore Machir the father of Gil'ad.
Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
15 And Machir took for wife [the sister] of Chuppim and Shuppim, whose sister's name was Ma'achah. And the name of the second was Zelophehad: and Zelophehad had daughters.
Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
16 And Ma'achah the wife of Machir bore a son, and she called his name Peresh; and the name of his brother was Sheresh; and his sons were Ulam and Rekem.
Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
17 And the sons of Ulam: Bedan. These were the sons of Gil'ad, the son of Machir, the son of Menasseh.
Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
18 And his sister Hammolecheth bore Isshod, and Abi'ezer, and Machlah.
Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
19 And the sons of Shemida' were, Achyan, and Shechem, and Likchi, and Ani'am.
Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
20 And the sons of Ephraim: Shuthelach, and Bered his son, and Tachath his son, and El'adah his son, and Tachath his son,
Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
21 And Zabad his son, and Shuthelach his son, and 'Ezer, and El'ad, whom the men of Gath that were born in that land slew, when they came down to take away their cattle.
Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
22 And Ephraim their father mourned many days, and his brethren came to comfort him.
Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
23 And he went in to his wife, and she conceived, and bore a son, and he called his name Beri'ah, because misfortune had come into his house.
Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
24 And his daughter was Sheerah, who built Beth-choron the lower, and the upper, and Uzzen-sheerah.
Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
25 And Rephach was his son, also Resheph, and Telach his son, and Tachan his son.
Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
26 La'dan his son, 'Ammihud his son, Elishama' his son,
Ladani, Amihudi, Elisama,
27 Non his son, Jehoshua' his son.
Nuni ndi Yoswa.
28 And their possessions and dwelling-places were, Beth-el and its villages, and at the east Na'aran, and at the west Gezer, with its villages, and Shechem with its villages, as far as Gazzah and its villages.
Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
29 And by the borders of the children of Menasseh: Beth-shean and its villages, Ta'nach and its villages, Megiddo and its villages, Dor and its villages. In these dwelt the children of Joseph the son of Israel.
Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
30 The sons of Asher: Yimnah, and Yishvah, and Yishvi, and Beri'ah, and Serach their sister.
Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
31 And the sons of Beri'ah: Cheber, and Malkiel, who is the father of Birzavith.
Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
32 And Cheber begat Yaphlet, and Shomer, and Chotham, and Shu'a their sister.
Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
33 And the sons of Yaphiet: Passach, and Bimhal, and 'Ashvath. These are the children of Yaphlet.
Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
34 And the sons of Shemer: Achi, and Rohgah, and Chubbah and Aram.
Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
35 And the sons of his brother Helem: Zophach, and Yimna', and Shelesh, and 'Amal
Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
36 The sons of Zophach: Suach, and Charnepher, and Shu'al, and Berl, and Yimrah,
Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
37 Bezer, and Hod, and Shamma, and Shilshah, and Yithran, and Beera.
Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
38 And the sons of Jether: Jephunneh, and Pisspah, and Ara.
Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
39 And the sons of 'Ulla: Arach, and Chaniel, and Rizya.
Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
40 All these were the children of Asher, heads of their family divisions, selected mighty men of valor, chiefs of the princes. And being recorded according to their genealogy for the army for the war, their number was of men twenty and six thousand.
Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.

< 1 Chronicles 7 >