< Psalms 59 >
1 For the end. Destroy not: by David for a memorial, when Saul sent, and watched his house to kill him. Deliver me from mine enemies, O God; and ransom me from those that rise up against me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Deliver me from the workers of iniquity, and save me from bloody men.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 For, behold, they have hunted after my soul; violent men have set upon me: neither [is it] my iniquity, nor my sin, O Lord.
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Without iniquity I ran and directed [my course aright]: awake to help me, and behold.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 And you, Lord God of hosts, the God of Israel, draw near to visit all the heathen; pity not any that work iniquity. (Pause)
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 They shall return at evening, and hunger like a dog, and go round about the city.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Behold, they shall utter a voice with their mouth, and a sword is in their lips; for who, [say they], has heard?
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 But you, Lord, will laugh them to scorn; you will utterly set at nothing all the heathen.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 will keep my strength, [looking] to you; for you, O God, are my helper.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 [As for] my God, his mercy shall go before me: my God will show me [vengeance] on mine enemies.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Slay them not, lest they forget your law; scatter them by your power; and bring them down, O Lord, my defender.
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 [For] the sin of their mouth, [and] the word of their lips, let them be even taken in their pride.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 And for [their] cursing and falsehood shall utter destruction be denounced: [they shall fall] by the wrath of utter destruction, and shall not be; so shall they know that the God of Jacob is Lord of the ends of the earth. (Pause)
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 They shall return at evening, and be hungry as a dog, and go round about the city.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 They shall be scattered hither and there for meat; and if they be not satisfied, they shall even murmur.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 But I will sing to your strength, and in the morning will I exult [in] your mercy; for you have been my supporter, and my refuge in the day of mine affliction.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 [You are] my helper; to you, my God, will I sing; you are my supporter, O my God, [and] my mercy.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.