< Psalms 127 >

1 A Song of Degrees. Except the Lord build the house, they that build labor in vain: except the Lord keep the city, the watchman watches in vain.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 It is vain for you to rise early: you rise up after resting, you that eat the bread of grief; while he gives sleep to his beloved.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 Behold, the inheritance of the Lord, children, the reward of the fruit of the womb.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 As arrows in the hand of a mighty man; so are the children of those who were outcasts.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Blessed is the man who shall satisfy his desire with them: they shall not be ashamed when they shall speak to their enemies in the gates.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

< Psalms 127 >