< Deuteronomy 13 >
1 And if there arise within you a prophet, or one who dreams a dream, and he gives you a sign or a wonder,
Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
2 and the sign or the wonder come to pass which he spoke to you, saying, Let us go and serve other gods, which you know not;
chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
3 you shall not listen to the words of that prophet, or the dreamer of that dream, because the Lord your God tries you, to know whether you love your God with all your heart and with all your soul.
musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
4 You shall follow the Lord your God, and fear him, and you shall hear his voice, and attach yourselves to him.
Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
5 And that prophet or that dreamer of a dream, shall die; for he has spoken to make you err from the Lord your God who brought you out of the land of Egypt, who redeemed you from bondage, to thrust you out of the way which the Lord your God commanded you to walk in: so shall you abolish the evil from among you.
Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
6 And if your brother by your father or mother, or your son, or daughter, or your wife in your bosom, or friend who is equal to your own soul, entreat you secretly, saying, Let us go and serve other gods, which neither you nor your fathers have known,
Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
7 of the gods of the nations that are round about you, who are near you or at a distance from you, from one end of the earth to the other;
milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
8 you shall not consent to him, neither shall you listen to him; and your eye shall not spare him, you shall feel no regret for him, neither shall you at all protect him:
musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
9 you shall surely report concerning him, and your hands shall be upon him among the first to kill him, and the hands of all the people at the last.
Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
10 And they shall stone him with stones, and he shall die, because he sought to draw you away from the Lord your God who brought you out of the land of Egypt, out of the house of bondage.
Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
11 And all Israel shall hear, and fear, and shall not again do according to this evil thing among you.
Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
12 And if in one of your cities which the Lord God gives you to dwell therein, you shall hear men saying,
Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
13 Evil men have gone out from you, and have caused all the inhabitants of their land to fall away, saying, Let us go and worship other gods, whom you knew not,
kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
14 then you shall enquire and ask, and search diligently, and behold, [if] the thing is clearly true, and this abomination has taken place among you,
mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
15 you shall utterly destroy all the dwellers in that land with the edge of the sword; you shall solemnly curse it, and all things in it.
muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
16 And all its spoils you shall gather into its public ways, and you shall burn the city with fire, and all its spoils publicly before the Lord your God; and it shall be uninhabited for ever, it shall not be built again.
Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
17 And there shall nothing of the cursed thing cleave to your hand, that the Lord may turn from his fierce anger, and show you mercy, and pity you, and multiply you, as he sware to your fathers;
Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
18 if you will hear the voice of the Lord your God, to keep his commandments, all that I charge you this day, to do that which is good and pleasing before the Lord your God.
chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.