< Psalms 128 >
1 A Song of degrees. Blessed [is] every one that feareth the LORD; that walketh in his ways.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 For thou shalt eat the labour of thine hands: happy [shalt] thou [be], and [it shall be] well with thee.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Thy wife [shall be] as a fruitful vine by the sides of thine house: thy children like olive plants round about thy table.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Behold, that thus shall the man be blessed that feareth the LORD.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 The LORD shall bless thee out of Zion: and thou shalt see the good of Jerusalem all the days of thy life.
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 Yea, thou shalt see thy children’s children, [and] peace upon Israel.
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.