< Psalms 67 >
1 God be merciful unto us, and bless us; and cause his face to shine upon us; (Selah)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 That your way may be known upon earth, your saving health among all nations.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Let the people praise you, O God; let all the people praise you.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 O let the nations be glad and sing for joy: for you shall judge the people righteously, and govern the nations upon earth. (Selah)
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Let the people praise you, O God; let all the people praise you.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Then shall the earth yield her increase; and God, even our own God, shall bless us.
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 God shall bless us; and all the ends of the earth shall fear him.
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.