< Psalms 44 >
1 We have heard with our ears, O God, our fathers have told us, what work you did in their days, in the times of old.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 How you did drive out the heathen with your hand, and planted them; how you did afflict the people, and cast them out.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 For they got not the land in possession by their own sword, neither did their own arm save them: but your right hand, and your arm, and the light of your countenance, because you had a favour unto them.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 You are my King, O God: command deliverances for Jacob.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Through you will we push down our enemies: through your name will we tread them under that rise up against us.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 For I will not trust in my bow, neither shall my sword save me.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 But you have saved us from our enemies, and have put them to shame that hated us.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 In God we boast all the day long, and praise your name for ever. (Selah)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 But you have cast off, and put us to shame; and go not forth with our armies.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 You make us to turn back from the enemy: and they which hate us spoil for themselves.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 You have given us like sheep appointed for food; and have scattered us among the heathen.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 You sell your people for nothing, and do not increase your wealth by their price.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 You make us a reproach to our neighbours, a scorn and a derision to them that are round about us.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 You make us a byword among the heathen, a shaking of the head among the people.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 My confusion is continually before me, and the shame of my face has covered me,
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 For the voice of him that reproaches and blasphemes; by reason of the enemy and avenger.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 All this has come upon us; yet have we not forgotten you, neither have we dealt falsely in your covenant.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Our heart is not turned back, neither have our steps declined from your way;
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Though you have sore broken us in the place of dragons, and covered us with the shadow of death.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 If we have forgotten the name of our God, or stretched out our hands to a strange god;
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Shall not God search this out? for he knows the secrets of the heart.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Yea, for your sake are we killed all the day long; we are counted as sheep for the slaughter.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Awake, why sleep you, O Lord? arise, cast us not off for ever.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Wherefore hide you your face, and forget our affliction and our oppression?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 For our soul is bowed down to the dust: our belly cleaves unto the earth.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Arise for our help, and redeem us for your mercies' sake.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.