< Psalms 12 >

1 Help, LORD; for the godly man ceases; for the faithful fail from among the children of men.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 They speak vanity every one with his neighbour: with flattering lips and with a double heart do they speak.
Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 The LORD shall cut off all flattering lips, and the tongue that speaks proud things:
Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 Who have said, With our tongue will we prevail; our lips are our own: who is lord over us?
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 For the oppression of the poor, for the sighing of the needy, now will I arise, says the LORD; I will set him in safety from him that puffs at him.
“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 The words of the LORD are pure words: as silver tried in a furnace of earth, purified seven times.
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 You shall keep them, O LORD, you shall preserve them from this generation for ever.
Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 The wicked walk on every side, when the vilest men are exalted.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.

< Psalms 12 >