< Psalms 94 >

1 O Yhwh God, to whom vengeance belongeth; O God, to whom vengeance belongeth, shew thyself.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Lift up thyself, thou judge of the earth: render a reward to the proud.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Yhwh, how long shall the wicked, how long shall the wicked triumph?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 How long shall they utter and speak hard things? and all the workers of iniquity boast themselves?
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 They break in pieces thy people, O Yhwh, and afflict thine heritage.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 They slay the widow and the stranger, and murder the fatherless.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Yet they say, Yah shall not see, neither shall the God of Jacob regard it.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Understand, ye brutish among the people: and ye fools, when will ye be wise?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 He that planted the ear, shall he not hear? he that formed the eye, shall he not see?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 He that chastiseth the heathen, shall not he correct? he that teacheth man knowledge, shall not he know?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Yhwh knoweth the thoughts of man, that they are vanity.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Blessed is the man whom thou chastenest, O Yah, and teachest him out of thy law;
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 That thou mayest give him rest from the days of adversity, until the pit be digged for the wicked.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 For Yhwh will not cast off his people, neither will he forsake his inheritance.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 But judgment shall return unto righteousness: and all the upright in heart shall follow it.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Who will rise up for me against the evildoers? or who will stand up for me against the workers of iniquity?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Unless Yhwh had been my help, my soul had almost dwelt in silence.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 When I said, My foot slippeth; thy mercy, O Yhwh, held me up.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 In the multitude of my thoughts within me thy comforts delight my soul.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Shall the throne of iniquity have fellowship with thee, which frameth mischief by a law?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 They gather themselves together against the soul of the righteous, and condemn the innocent blood.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 But Yhwh is my defence; and my God is the rock of my refuge.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 And he shall bring upon them their own iniquity, and shall cut them off in their own wickedness; yea, Yhwh our God shall cut them off.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psalms 94 >