< Psalms 66 >
1 Make a joyful noise unto God, all ye lands:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Sing forth the honour of his name: make his praise glorious.
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Say unto God, How terrible art thou in thy works! through the greatness of thy power shall thine enemies submit themselves unto thee.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 All the earth shall worship thee, and shall sing unto thee; they shall sing to thy name. (Selah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Come and see the works of God: he is terrible in his doing toward the children of men.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 He turned the sea into dry land: they went through the flood on foot: there did we rejoice in him.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 He ruleth by his power for ever; his eyes behold the nations: let not the rebellious exalt themselves. (Selah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 O bless our God, ye people, and make the voice of his praise to be heard:
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 Which holdeth our soul in life, and suffereth not our feet to be moved.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 For thou, O God, hast proved us: thou hast tried us, as silver is tried.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 Thou broughtest us into the net; thou laidst affliction upon our loins.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 Thou hast caused men to ride over our heads; we went through fire and through water: but thou broughtest us out into a place of abundance.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 I will go into thy house with burnt offerings: I will pay thee my vows,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Which my lips have uttered, and my mouth hath spoken, when I was in trouble.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 I will offer unto thee burnt sacrifices of fatlings, with the incense of rams; I will offer bullocks with goats. (Selah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Come and hear, all ye that fear God, and I will declare what he hath done for my soul.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 I cried unto him with my mouth, and he was extolled with my tongue.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 If I regard iniquity in my heart, the Lord will not hear me:
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 But verily God hath heard me; he hath attended to the voice of my prayer.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Blessed be God, which hath not turned away my prayer, nor his mercy from me.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!