< Psalms 6 >

1 O Yhwh, rebuke me not in thine anger, neither chasten me in thy hot displeasure.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Have mercy upon me, O Yhwh; for I am weak: O Yhwh, heal me; for my bones are vexed.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 My soul is also sore vexed: but thou, O Yhwh, how long?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Return, O Yhwh, deliver my soul: oh save me for thy mercies’ sake.
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For in death there is no remembrance of thee: in the grave who shall give thee thanks? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 I am weary with my groaning; all the night make I my bed to swim; I water my couch with my tears.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Mine eye is consumed because of grief; it waxeth old because of all mine enemies.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Depart from me, all ye workers of iniquity; for Yhwh hath heard the voice of my weeping.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Yhwh hath heard my supplication; Yhwh will receive my prayer.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Let all mine enemies be ashamed and sore vexed: let them return and be ashamed suddenly.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalms 6 >