< Psalms 54 >
1 Save me, O God, by thy name, and judge me by thy strength.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Hear my prayer, O God; give ear to the words of my mouth.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 For strangers are risen up against me, and oppressors seek after my soul: they have not set God before them. (Selah)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Behold, God is mine helper: the Lord is with them that uphold my soul.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 He shall reward evil unto mine enemies: cut them off in thy truth.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 I will freely sacrifice unto thee: I will praise thy name, O Yhwh; for it is good.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 For he hath delivered me out of all trouble: and mine eye hath seen his desire upon mine enemies.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.