< Psalms 129 >
1 Many a time have they afflicted me from my youth, may Israel now say:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 Many a time have they afflicted me from my youth: yet they have not prevailed against me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 The plowers plowed upon my back: they made long their furrows.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 Yhwh is righteous: he hath cut asunder the cords of the wicked.
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Let them all be confounded and turned back that hate Zion.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Let them be as the grass upon the housetops, which withereth afore it groweth up:
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 Wherewith the mower filleth not his hand; nor he that bindeth sheaves his bosom.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 Neither do they which go by say, The blessing of Yhwh be upon you: we bless you in the name of Yhwh.
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”