< Proverbs 23 >
1 When thou sittest to eat with a ruler, consider diligently what is before thee:
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 And put a knife to thy throat, if thou be a man given to appetite.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Be not desirous of his dainties: for they are deceitful meat.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Labour not to be rich: cease from thine own wisdom.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Wilt thou set thine eyes upon that which is not? for riches certainly make themselves wings; they fly away as an eagle toward heaven.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Eat thou not the bread of him that hath an evil eye, neither desire thou his dainty meats:
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 For as he thinketh in his heart, so is he: Eat and drink, saith he to thee; but his heart is not with thee.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 The morsel which thou hast eaten shalt thou vomit up, and lose thy sweet words.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Speak not in the ears of a fool: for he will despise the wisdom of thy words.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Remove not the old landmark; and enter not into the fields of the fatherless:
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 For their redeemer is mighty; he shall plead their cause with thee.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Apply thine heart unto instruction, and thine ears to the words of knowledge.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Withhold not correction from the child: for if thou beatest him with the rod, he shall not die.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Thou shalt beat him with the rod, and shalt deliver his soul from hell. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
15 My son, if thine heart be wise, my heart shall rejoice, even mine.
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Yea, my reins shall rejoice, when thy lips speak right things.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Let not thine heart envy sinners: but be thou in the fear of Yhwh all the day long.
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 For surely there is an end; and thine expectation shall not be cut off.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Hear thou, my son, and be wise, and guide thine heart in the way.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Be not among winebibbers; among riotous eaters of flesh:
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For the drunkard and the glutton shall come to poverty: and drowsiness shall clothe a man with rags.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Hearken unto thy father that begat thee, and despise not thy mother when she is old.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Buy the truth, and sell it not; also wisdom, and instruction, and understanding.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 The father of the righteous shall greatly rejoice: and he that begetteth a wise child shall have joy of him.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Thy father and thy mother shall be glad, and she that bare thee shall rejoice.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 My son, give me thine heart, and let thine eyes observe my ways.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 For a whore is a deep ditch; and a strange woman is a narrow pit.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 She also lieth in wait as for a prey, and increaseth the transgressors among men.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Who hath woe? who hath sorrow? who hath contentions? who hath babbling? who hath wounds without cause? who hath redness of eyes?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 They that tarry long at the wine; they that go to seek mixed wine.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Look not thou upon the wine when it is red, when it giveth his colour in the cup, when it moveth itself aright.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 At the last it biteth like a serpent, and stingeth like an adder.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Thine eyes shall behold strange women, and thine heart shall utter perverse things.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Yea, thou shalt be as he that lieth down in the midst of the sea, or as he that lieth upon the top of a mast.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 They have stricken me, shalt thou say, and I was not sick; they have beaten me, and I felt it not: when shall I awake? I will seek it yet again.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”