< Job 14 >

1 Man that is born of a woman is of few days, and full of trouble.
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 He cometh forth like a flower, and is cut down: he fleeth also as a shadow, and continueth not.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 And dost thou open thine eyes upon such an one, and bringest me into judgment with thee?
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 Who can bring a clean thing out of an unclean? not one.
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Seeing his days are determined, the number of his months are with thee, thou hast appointed his bounds that he cannot pass;
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Turn from him, that he may rest, till he shall accomplish, as an hireling, his day.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 For there is hope of a tree, if it be cut down, that it will sprout again, and that the tender branch thereof will not cease.
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Though the root thereof wax old in the earth, and the stock thereof die in the ground;
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 Yet through the scent of water it will bud, and bring forth boughs like a plant.
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 But man dieth, and wasteth away: yea, man giveth up the ghost, and where is he?
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 As the waters fail from the sea, and the flood decayeth and drieth up:
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 So man lieth down, and riseth not: till the heavens be no more, they shall not awake, nor be raised out of their sleep.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 O that thou wouldest hide me in the grave, that thou wouldest keep me secret, until thy wrath be past, that thou wouldest appoint me a set time, and remember me! (Sheol h7585)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
14 If a man die, shall he live again? all the days of my appointed time will I wait, till my change come.
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Thou shalt call, and I will answer thee: thou wilt have a desire to the work of thine hands.
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 For now thou numberest my steps: dost thou not watch over my sin?
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 My transgression is sealed up in a bag, and thou sewest up mine iniquity.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 And surely the mountain falling cometh to nought, and the rock is removed out of his place.
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 The waters wear the stones: thou washest away the things which grow out of the dust of the earth; and thou destroyest the hope of man.
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Thou prevailest for ever against him, and he passeth: thou changest his countenance, and sendest him away.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 His sons come to honour, and he knoweth it not; and they are brought low, but he perceiveth it not of them.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 But his flesh upon him shall have pain, and his soul within him shall mourn.
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

< Job 14 >