< Psalms 71 >

1 In thee, O YHWH, do I put my trust: let me never be put to confusion.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Deliver me in thy righteousness, and cause me to escape: incline thine ear unto me, and save me.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Be thou my strong habitation, whereunto I may continually resort: thou hast given commandment to save me; for thou art my rock and my fortress.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Deliver me, O my Elohim, out of the hand of the wicked, out of the hand of the unrighteous and cruel man.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 For thou art my hope, O Sovereign YHWH: thou art my trust from my youth.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 By thee have I been holden up from the womb: thou art he that took me out of my mother's bowels: my praise shall be continually of thee.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 I am as a wonder unto many; but thou art my strong refuge.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Let my mouth be filled with thy praise and with thy honour all the day.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Cast me not off in the time of old age; forsake me not when my strength faileth.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 For mine enemies speak against me; and they that lay wait for my soul take counsel together,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Saying, Elohim hath forsaken him: persecute and take him; for there is none to deliver him.
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 O Elohim, be not far from me: O my Elohim, make haste for my help.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Let them be confounded and consumed that are adversaries to my soul; let them be covered with reproach and dishonour that seek my hurt.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 But I will hope continually, and will yet praise thee more and more.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 My mouth shall shew forth thy righteousness and thy salvation all the day; for I know not the numbers thereof.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 I will go in the strength of the Sovereign YHWH: I will make mention of thy righteousness, even of thine only.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 O Elohim, thou hast taught me from my youth: and hitherto have I declared thy wondrous works.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Now also when I am old and grayheaded, O Elohim, forsake me not; until I have shewed thy strength unto this generation, and thy power to every one that is to come.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Thy righteousness also, O Elohim, is very high, who hast done great things: O Elohim, who is like unto thee!
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Thou, which hast shewed me great and sore troubles, shalt quicken me again, and shalt bring me up again from the depths of the earth.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Thou shalt increase my greatness, and comfort me on every side.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 I will also praise thee with the psaltery, even thy truth, O my Elohim: unto thee will I sing with the harp, O thou Holy One of Israel.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 My lips shall greatly rejoice when I sing unto thee; and my soul, which thou hast redeemed.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 My tongue also shall talk of thy righteousness all the day long: for they are confounded, for they are brought unto shame, that seek my hurt.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Psalms 71 >