< Psalms 14 >

1 The fool hath said in his heart, There is no Elohim. They are corrupt, they have done abominable works, there is none that doeth good.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
2 YHWH looked down from heaven upon the children of men, to see if there were any that did understand, and seek Elohim.
Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
3 They are all gone aside, they are all together become filthy: there is none that doeth good, no, not one.
Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Have all the workers of iniquity no knowledge? who eat up my people as they eat bread, and call not upon YHWH.
Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
5 There were they in great fear: for Elohim is in the generation of the righteous.
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 Ye have shamed the counsel of the poor, because YHWH is his refuge.
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 Oh that the salvation of Israel were come out of Zion! when YHWH bringeth back the captivity of his people, Jacob shall rejoice, and Israel shall be glad.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

< Psalms 14 >