< Job 3 >

1 After this opened Job his mouth, and cursed his day.
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 And Job spake, and said,
Ndipo Yobu anati:
3 Let the day perish wherein I was born, and the night in which it was said, There is a man child conceived.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Let that day be darkness; let not Eloah regard it from above, neither let the light shine upon it.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Let darkness and the shadow of death stain it; let a cloud dwell upon it; let the blackness of the day terrify it.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 As for that night, let darkness seize upon it; let it not be joined unto the days of the year, let it not come into the number of the months.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Lo, let that night be solitary, let no joyful voice come therein.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Let them curse it that curse the day, who are ready to raise up their mourning.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Let the stars of the twilight thereof be dark; let it look for light, but have none; neither let it see the dawning of the day:
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Because it shut not up the doors of my mother's womb, nor hid sorrow from mine eyes.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Why died I not from the womb? why did I not give up the ghost when I came out of the belly?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Why did the knees prevent me? or why the breasts that I should suck?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 For now should I have lain still and been quiet, I should have slept: then had I been at rest,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 With kings and counsellers of the earth, which built desolate places for themselves;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 Or with princes that had gold, who filled their houses with silver:
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Or as an hidden untimely birth I had not been; as infants which never saw light.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There the wicked cease from troubling; and there the weary be at rest.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 There the prisoners rest together; they hear not the voice of the oppressor.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 The small and great are there; and the servant is free from his master.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Wherefore is light given to him that is in misery, and life unto the bitter in soul;
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 Which long for death, but it cometh not; and dig for it more than for hid treasures;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 Which rejoice exceedingly, and are glad, when they can find the grave?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Why is light given to a man whose way is hid, and whom Eloah hath hedged in?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 For my sighing cometh before I eat, and my roarings are poured out like the waters.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 For the thing which I greatly feared is come upon me, and that which I was afraid of is come unto me.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 I was not in safety, neither had I rest, neither was I quiet; yet trouble came.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >