< Psalms 147 >

1 PRAISE ye the Lord: for it is good to sing praises unto our God; for it is pleasant; and praise is comely.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 The Lord doth build up Jerusalem: he gathereth together the outcasts of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 He healeth the broken in heart, and bindeth up their wounds.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 He telleth the number of the stars; he calleth them all by their names.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Great is our Lord, and of great power: his understanding is infinite.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 The Lord lifteth up the meek: he casteth the wicked down to the ground.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Sing unto the Lord with thanksgiving; sing praise upon the harp unto our God:
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Who covereth the heaven with clouds, who prepareth rain for the earth, who maketh grass to grow upon the mountains.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 He giveth to the beast his food, and to the young ravens which cry.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He delighteth not in the strength of the horse: he taketh not pleasure in the legs of a man.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 The Lord taketh pleasure in them that fear him, in those that hope in his mercy.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Praise the Lord, O Jerusalem; praise thy God, O Zion.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For he hath strengthened the bars of thy gates; he hath blessed thy children within thee.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 He maketh peace in thy borders, and filleth thee with the finest of the wheat.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 He sendeth forth his commandment upon earth: his word runneth very swiftly.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 He giveth snow like wool: he scattereth the hoarfrost like ashes.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He casteth forth his ice like morsels: who can stand before his cold?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He sendeth out his word, and melteth them: he causeth his wind to blow, and the waters flow.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 He sheweth his word unto Jacob, his statutes and his judgments unto Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He hath not dealt so with any nation: and as for his judgments, they have not known them. Praise ye the Lord.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 147 >