< Psalms 104 >

1 BLESS the Lord, O my soul. O Lord my God, thou art very great; thou art clothed with honour and majesty.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Who coverest thyself with light as with a garment: who stretchest out the heavens like a curtain:
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 Who layeth the beams of his chambers in the waters: who maketh the clouds his chariot: who walketh upon the wings of the wind:
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Who maketh his angels spirits; his ministers a flaming fire:
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Who laid the foundations of the earth, that it should not be removed for ever.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Thou coveredst it with the deep as with a garment: the waters stood above the mountains.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 At thy rebuke they fled; at the voice of thy thunder they hasted away.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 They go up by the mountains; they go down by the valleys unto the place which thou hast founded for them.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Thou hast set a bound that they may not pass over; that they turn not again to cover the earth.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 He sendeth the springs into the valleys, which run among the hills.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 They give drink to every beast of the field: the wild asses quench their thirst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 By them shall the fowls of the heaven have their habitation, which sing among the branches.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 He watereth the hills from his chambers: the earth is satisfied with the fruit of thy works.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 He causeth the grass to grow for the cattle, and herb for the service of man: that he may bring forth food out of the earth;
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 And wine that maketh glad the heart of man, and oil to make his face to shine, and bread which strengtheneth man’s heart.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 The trees of the Lord are full of sap; the cedars of Lebanon, which he hath planted;
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 Where the birds make their nests: as for the stork, the fir trees are her house.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 The high hills are a refuge for the wild goats; and the rocks for the conies.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 He appointed the moon for seasons: the sun knoweth his going down.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Thou makest darkness, and it is night: wherein all the beasts of the forest do creep forth.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 The young lions roar after their prey, and seek their meat from God.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 The sun ariseth, they gather themselves together, and lay them down in their dens.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Man goeth forth unto his work and to his labour until the evening.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 O Lord, how manifold are thy works! in wisdom hast thou made them all: the earth is full of thy riches.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 So is this great and wide sea, wherein are things creeping innumerable, both small and great beasts.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 There go the ships: there is that leviathan, whom thou hast made to play therein.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 These wait all upon thee; that thou mayest give them their meat in due season.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 That thou givest them they gather: thou openest thine hand, they are filled with good.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Thou hidest thy face, they are troubled: thou takest away their breath, they die, and return to their dust.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Thou sendest forth thy spirit, they are created: and thou renewest the face of the earth.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 The glory of the Lord shall endure for ever: the Lord shall rejoice in his works.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 He looketh on the earth, and it trembleth: he toucheth the hills, and they smoke.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 I will sing unto the Lord as long as I live: I will sing praise to my God while I have my being.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 My meditation of him shall be sweet: I will be glad in the Lord.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Let the sinners be consumed out of the earth, and let the wicked be no more. Bless thou the Lord, O my soul. Praise ye the Lord.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalms 104 >