< Proverbs 19 >

1 BETTER is the poor that walketh in his integrity, than he that is perverse in his lips, and is a fool.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 Also, that the soul be without knowledge, it is not good; and he that hasteth with his feet sinneth.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 The foolishness of man perverteth his way: and his heart fretteth against the Lord.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Wealth maketh many friends; but the poor is separated from his neighbour.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 A false witness shall not be unpunished, and he that speaketh lies shall not escape.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Many will intreat the favour of the prince: and every man is a friend to him that giveth gifts.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 All the brethren of the poor do hate him: how much more do his friends go far from him? he pursueth them with words, yet they are wanting to him.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 He that getteth wisdom loveth his own soul: he that keepeth understanding shall find good.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 A false witness shall not be unpunished, and he that speaketh lies shall perish.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Delight is not seemly for a fool; much less for a servant to have rule over princes.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 The discretion of a man deferreth his anger; and it is his glory to pass over a transgression.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 The king’s wrath is as the roaring of a lion; but his favour is as dew upon the grass.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 A foolish son is the calamity of his father: and the contentions of a wife are a continual dropping.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 House and riches are the inheritance of fathers: and a prudent wife is from the Lord.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Slothfulness casteth into a deep sleep; and an idle soul shall suffer hunger.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 He that keepeth the commandment keepeth his own soul; but he that despiseth his ways shall die.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 He that hath pity upon the poor lendeth unto the Lord; and that which he hath given will he pay him again.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Chasten thy son while there is hope, and let not thy soul spare for his crying.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 A man of great wrath shall suffer punishment: for if thou deliver him, yet thou must do it again.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Hear counsel, and receive instruction, that thou mayest be wise in thy latter end.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 There are many devices in a man’s heart; nevertheless the counsel of the Lord, that shall stand.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 The desire of a man is his kindness: and a poor man is better than a liar.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 The fear of the Lord tendeth to life: and he that hath it shall abide satisfied; he shall not be visited with evil.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 A slothful man hideth his hand in his bosom, and will not so much as bring it to his mouth again.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Smite a scorner, and the simple will beware: and reprove one that hath understanding, and he will understand knowledge.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 He that wasteth his father, and chaseth away his mother, is a son that causeth shame, and bringeth reproach.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Cease, my son, to hear the instruction that causeth to err from the words of knowledge.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 An ungodly witness scorneth judgment: and the mouth of the wicked devoureth iniquity.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Judgments are prepared for scorners, and stripes for the back of fools.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Proverbs 19 >