< Psalms 48 >
1 Great is the LORD, and greatly to be praised in the city of our God, in the mountain of his holiness.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Beautiful for situation, the joy of the whole earth, is mount Zion, on the sides of the north, the city of the great King.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 God is known in her palaces for a refuge.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 For, see, the kings were assembled, they passed by together.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 They saw it, and so they marveled; they were troubled, and hurried away.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Fear took hold on them there, and pain, as of a woman in travail.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 You break the ships of Tarshish with an east wind.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 As we have heard, so have we seen in the city of the LORD of hosts, in the city of our God: God will establish it for ever. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 We have thought of your loving kindness, O God, in the middle of your temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 According to your name, O God, so is your praise to the ends of the earth: your right hand is full of righteousness.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Let mount Zion rejoice, let the daughters of Judah be glad, because of your judgments.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Walk about Zion, and go round about her: tell the towers thereof.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Mark you well her bulwarks, consider her palaces; that you may tell it to the generation following.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 For this God is our God for ever and ever: he will be our guide even to death.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.