< Psalms 45 >
1 My heart is gushing a good matter: I speak of the things which I have made touching the king: my tongue is the pen of a ready writer.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 You are fairer than the children of men: grace is poured into your lips: therefore God has blessed you for ever.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Gird your sword on your thigh, O most mighty, with your glory and your majesty.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 And in your majesty ride prosperously because of truth and meekness and righteousness; and your right hand shall teach you terrible things.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Your arrows are sharp in the heart of the king’s enemies; whereby the people fall under you.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Your throne, O God, is for ever and ever: the scepter of your kingdom is a right scepter.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 You love righteousness, and hate wickedness: therefore God, your God, has anointed you with the oil of gladness above your fellows.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 All your garments smell of myrrh, and aloes, and cassia, out of the ivory palaces, whereby they have made you glad.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Kings’ daughters were among your honorable women: on your right hand did stand the queen in gold of Ophir.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Listen, O daughter, and consider, and incline your ear; forget also your own people, and your father’s house;
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 So shall the king greatly desire your beauty: for he is your Lord; and worship you him.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 And the daughter of Tyre shall be there with a gift; even the rich among the people shall entreat your favor.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 The king’s daughter is all glorious within: her clothing is of worked gold.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 She shall be brought to the king in raiment of needlework: the virgins her companions that follow her shall be brought to you.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 With gladness and rejoicing shall they be brought: they shall enter into the king’s palace.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Instead of your fathers shall be your children, whom you may make princes in all the earth.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 I will make your name to be remembered in all generations: therefore shall the people praise you for ever and ever.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.