< Psalms 141 >

1 Lord, I cry to you: make haste to me; give ear to my voice, when I cry to you.
Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 Let my prayer be set forth before you as incense; and the lifting up of my hands as the evening sacrifice.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Set a watch, O LORD, before my mouth; keep the door of my lips.
Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Incline not my heart to any evil thing, to practice wicked works with men that work iniquity: and let me not eat of their dainties.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 Let the righteous smite me; it shall be a kindness: and let him reprove me; it shall be an excellent oil, which shall not break my head: for yet my prayer also shall be in their calamities.
Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 When their judges are overthrown in stony places, they shall hear my words; for they are sweet.
Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 Our bones are scattered at the grave’s mouth, as when one cuts and splits wood on the earth. (Sheol h7585)
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
8 But my eyes are to you, O GOD the Lord: in you is my trust; leave not my soul destitute.
Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Keep me from the snares which they have laid for me, and the gins of the workers of iniquity.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Let the wicked fall into their own nets, whilst that I with escape.
Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

< Psalms 141 >