< Psalms 114 >
1 When Israel went out of Egypt, the house of Jacob from a people of strange language;
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judah was his sanctuary, and Israel his dominion.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The sea saw it, and fled: Jordan was driven back.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 The mountains skipped like rams, and the little hills like lambs.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 What ailed you, O you sea, that you fled? you Jordan, that you were driven back?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 You mountains, that you skipped like rams; and you little hills, like lambs?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Tremble, you earth, at the presence of the Lord, at the presence of the God of Jacob;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Which turned the rock into a standing water, the flint into a fountain of waters.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.