< Numbers 17 >

1 And the LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak to the children of Israel, and take of every one of them a rod according to the house of their fathers, of all their princes according to the house of their fathers twelve rods: write you every man’s name on his rod.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
3 And you shall write Aaron’s name on the rod of Levi: for one rod shall be for the head of the house of their fathers.
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
4 And you shall lay them up in the tabernacle of the congregation before the testimony, where I will meet with you.
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
5 And it shall come to pass, that the man’s rod, whom I shall choose, shall blossom: and I will make to cease from me the murmurings of the children of Israel, whereby they murmur against you.
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
6 And Moses spoke to the children of Israel, and every one of their princes gave him a rod apiece, for each prince one, according to their fathers’ houses, even twelve rods: and the rod of Aaron was among their rods.
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
7 And Moses laid up the rods before the LORD in the tabernacle of witness.
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
8 And it came to pass, that on the morrow Moses went into the tabernacle of witness; and, behold, the rod of Aaron for the house of Levi was budded, and brought forth buds, and bloomed blossoms, and yielded almonds.
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
9 And Moses brought out all the rods from before the LORD to all the children of Israel: and they looked, and took every man his rod.
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
10 And the LORD said to Moses, Bring Aaron’s rod again before the testimony, to be kept for a token against the rebels; and you shall quite take away their murmurings from me, that they die not.
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
11 And Moses did so: as the LORD commanded him, so did he.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
12 And the children of Israel spoke to Moses, saying, Behold, we die, we perish, we all perish.
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
13 Whoever comes any thing near to the tabernacle of the LORD shall die: shall we be consumed with dying?
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

< Numbers 17 >