< Zechariah 5 >

1 Then again I lifted up mine eyes, and saw, and behold a flying roll.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 And he said unto me: 'What seest thou?' And I answered: 'I see a flying roll; the length thereof is twenty cubits, and the breadth thereof ten cubits.'
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Then said he unto me: 'This is the curse that goeth forth over the face of the whole land; for every one that stealeth shall be swept away on the one side like it; and every one that sweareth shall be swept away on the other side like it.
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 I cause it to go forth, saith the LORD of hosts, and it shall enter into the house of the thief, and into the house of him that sweareth falsely by My name; and it shall abide in the midst of his house, and shall consume it with the timber thereof and the stones thereof.'
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 Then the angel that spoke with me went forth, and said unto me: 'Lift up now thine eyes, and see what is this that goeth forth.'
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 And I said: 'What is it?' And he said: 'This is the measure that goeth forth.' He said moreover: 'This is their eye in all the land —
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 and, behold, there was lifted up a round piece of lead — and this is a woman sitting in the midst of the measure.'
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 And he said: 'This is Wickedness.' And he cast her down into the midst of the measure, and he cast the weight of lead upon the mouth thereof.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Then lifted I up mine eyes, and saw, and, behold, there came forth two women, and the wind was in their wings; for they had wings like the wings of a stork; and they lifted up the measure between the earth and the heaven.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Then said I to the angel that spoke with me: 'Whither do these bear the measure?'
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 And he said unto me: 'To build her a house in the land of Shinar; and when it is prepared, she shall be set there in her own place.
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

< Zechariah 5 >