< Song of Solomon 6 >

1 'Whither is thy beloved gone, O thou fairest among women? Whither hath thy beloved turned him, that we may seek him with thee?'
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti? Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
2 'My beloved is gone down into his garden, to the beds of spices, to feed in the gardens, and to gather lilies.
Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake, ku timinda ta zokometsera zakudya, akukadyetsa ziweto zake ku minda, ndiponso akuthyola maluwa okongola.
3 I am my beloved's, and my beloved is mine, that feedeth among the lilies.'
Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga; amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
4 Thou art beautiful, O my love, as Tirzah, comely as Jerusalem, terrible as an army with banners.
Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
5 Turn away thine eyes from me, for they have overcome me. Thy hair is as a flock of goats, that trail down from Gilead.
Usandipenyetsetse; pakuti maso ako amanditenga mtima. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
6 Thy teeth are like a flock of ewes, which are come up from the washing; whereof all are paired, and none faileth among them.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa, iliyonse ili ndi ana amapasa, palibe imene ili yokha.
7 Thy temples are like a pomegranate split open behind thy veil.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu, masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
8 There are threescore queens, and fourscore concubines, and maidens without number.
Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60, ndi azikazi 80, ndi anamwali osawerengeka;
9 My dove, my undefiled, is but one; she is the only one of her mother; she is the choice one of her that bore her. The daughters saw her, and called her happy; yea, the queens and the concubines, and they praised her.
koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense; mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake, mwana wapamtima wa amene anamubereka. Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala; akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
10 Who is she that looketh forth as the dawn, fair as the moon, clear as the sun, terrible as an army with banners?
Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha, wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa, wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
11 I went down into the garden of nuts, to look at the green plants of the valley, to see whether the vine budded, and the pomegranates were in flower.
Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa, kukaona ngati mpesa waphukira kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Before I was aware, my soul set me upon the chariots of my princely people.
Ndisanazindikire kanthu, ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
13 Return, return, O Shulammite; Return, return, that we may look upon thee. What will ye see in the Shulammite? As it were a dance of two companies.
Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami; bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe! Mwamuna Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami, pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

< Song of Solomon 6 >