< Psalms 94 >
1 O LORD, Thou God to whom vengeance belongeth, Thou God to whom vengeance belongeth, shine forth.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Lift up Thyself, Thou Judge of the earth; render to the proud their recompense.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 LORD, how long shall the wicked, how long shall the wicked exult?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 They gush out, they speak arrogancy; all the workers of iniquity bear themselves loftily.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 They crush Thy people, O LORD, and afflict Thy heritage.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 They slay the widow and the stranger, and murder the fatherless.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 And they say: 'The LORD will not see, neither will the God of Jacob give heed.'
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Consider, ye brutish among the people; and ye fools, when will ye understand?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 He that planted the ear, shall He not hear? He that formed the eye, shall He not see?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 He that instructeth nations, shall not He correct? even He that teacheth man knowledge?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 The LORD knoweth the thoughts of man, that they are vanity.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Happy is the man whom Thou instructest, O LORD, and teachest out of Thy law;
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 That Thou mayest give him rest from the days of evil, until the pit be digged for the wicked.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 For the LORD will not cast off His people, neither will He forsake His inheritance.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 For right shall return unto justice, and all the upright in heart shall follow it.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Who will rise up for me against the evil-doers? Who will stand up for me against the workers of iniquity?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Unless the LORD had been my help, my soul had soon dwelt in silence.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 If I say: 'My foot slippeth', Thy mercy, O LORD, holdeth me up.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 When my cares are many within me, Thy comforts delight my soul.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Shall the seat of wickedness have fellowship with Thee, which frameth mischief by statute?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 They gather themselves together against the soul of the righteous, and condemn innocent blood.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 But the LORD hath been my high tower, and my God the rock of my refuge.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 And He hath brought upon them their own iniquity, and will cut them off in their own evil; the LORD our God will cut them off.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.