< Psalms 9 >

1 For the Leader; upon Muthlabben. A Psalm of David. I will give thanks unto the LORD with my whole heart; I will tell of all Thy marvellous works.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 I will be glad and exult in Thee; I will sing praise to Thy name, O Most High:
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 When mine enemies are turned back, they stumble and perish at Thy presence;
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 For Thou hast maintained my right and my cause; Thou sattest upon the throne as the righteous Judge.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Thou hast rebuked the nations, Thou hast destroyed the wicked, Thou hast blotted out their name for ever and ever.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 O thou enemy, the waste places are come to an end for ever; and the cities which thou didst uproot, their very memorial is perished.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 But the LORD is enthroned for ever; He hath established His throne for judgment.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 And He will judge the world in righteousness, He will minister judgment to the peoples with equity.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 The LORD also will be a high tower for the oppressed, a high tower in times of trouble;
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 And they that know Thy name will put their trust in Thee; for thou, LORD, hast not forsaken them that seek Thee.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Sing praises to the LORD, who dwelleth in Zion; declare among the peoples His doings.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 For He that avengeth blood hath remembered them; He hath not forgotten the cry of the humble.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Be gracious unto me, O LORD, behold mine affliction at the hands of them that hate me; Thou that liftest me up from the gates of death;
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 That I may tell of all Thy praise in the gates of the daughter of Zion, that I may rejoice in Thy salvation.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 The nations are sunk down in the pit that they made; in the net which they hid is their own foot taken.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 The LORD hath made Himself known, He hath executed judgment, the wicked is snared in the work of his own hands. (Higgaion, Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 The wicked shall return to the nether-world, even all the nations that forget God. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 For the needy shall not alway be forgotten, nor the expectation of the poor perish for ever.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Arise, O LORD, let not man prevail; let the nations be judged in Thy sight.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Set terror over them, O LORD; let the nations know they are but men. (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Psalms 9 >