< Psalms 85 >

1 For the Leader. A Psalm of the sons of Korah. LORD, Thou hast been favourable unto Thy land, Thou hast turned the captivity of Jacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Thou hast forgiven the iniquity of Thy people, Thou hast pardoned all their sin. (Selah)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Thou hast withdrawn all Thy wrath; Thou hast turned from the fierceness of Thine anger.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Restore us, O God of our salvation, and cause Thine indignation toward us to cease.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Wilt Thou be angry with us for ever? Wilt Thou draw out Thine anger to all generations?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Wilt Thou not quicken us again, that Thy people may rejoice in Thee?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Show us Thy mercy, O LORD, and grant us Thy salvation.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 I will hear what God the LORD will speak; for He will speak peace unto His people, and to His saints; but let them not turn back to folly.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Surely His salvation is nigh them that fear Him; that glory may dwell in our land.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Mercy and truth are met together; righteousness and peace have kissed each other.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Truth springeth out of the earth; and righteousness hath looked down from heaven.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Yea, the LORD will give that which is good; and our land shall yield her produce.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Righteousness shall go before Him, and shall make His footsteps a way.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalms 85 >