< Psalms 80 >

1 For the Leader; upon Shoshannim. A testimony. A Psalm of Asaph. Give ear, O Shepherd of Israel, Thou that leadest Joseph like a flock; Thou that art enthroned upon the cherubim, shine forth.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Before Ephraim and Benjamin and Manasseh, stir up Thy might, and come to save us.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 O God, restore us; and cause Thy face to shine, and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 O LORD God of hosts, how long wilt Thou be angry against the prayer of Thy people?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Thou hast fed them with the bread of tears, and given them tears to drink in large measure.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Thou makest us a strife unto our neighbours; and our enemies mock as they please.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 O God of hosts, restore us; and cause Thy face to shine, and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 Thou didst pluck up a vine out of Egypt; Thou didst drive out the nations, and didst plant it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 Thou didst clear a place before it, and it took deep root, and filled the land.
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 The mountains were covered with the shadow of it, and the mighty cedars with the boughs thereof.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 She sent out her branches unto the sea, and her shoots unto the River.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Why hast Thou broken down her fences, so that all they that pass by the way do pluck her?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 The boar out of the wood doth ravage it, that which moveth in the field feedeth on it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 O God of hosts, return, we beseech Thee; look from heaven, and behold, and be mindful of this vine,
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 And of the stock which Thy right hand hath planted, and the branch that Thou madest strong for Thyself.
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 It is burned with fire, it is cut down; they perish at the rebuke of Thy countenance.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Let Thy hand be upon the man of Thy right hand, upon the son of man whom Thou madest strong for Thyself.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 So shall we not turn back from Thee; quicken Thou us, and we will call upon Thy name.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 O LORD God of hosts, restore us; cause Thy face to shine, and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.

< Psalms 80 >