< Psalms 74 >

1 Maschil of Asaph. Why, O God, hast Thou cast us off for ever? Why doth Thine anger smoke against the flock of Thy pasture?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Remember Thy congregation, which Thou hast gotten of old, which Thou hast redeemed to be the tribe of Thine inheritance; and mount Zion, wherein Thou hast dwelt.
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Lift up Thy steps because of the perpetual ruins, even all the evil that the enemy hath done in the sanctuary.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Thine adversaries have roared in the midst of Thy meeting-place; they have set up their own signs for signs.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 It seemed as when men wield upwards axes in a thicket of trees.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 And now all the carved work thereof together they strike down with hatchet and hammers.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 They have set Thy sanctuary on fire; they have profaned the dwelling-place of Thy name even to the ground.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 They said in their heart: 'Let us make havoc of them altogether'; they have burned up all the meeting-places of God in the land.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 We see not our signs; there is no more any prophet; neither is there among us any that knoweth how long.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 How long, O God, shall the adversary reproach? Shall the enemy blaspheme Thy name for ever?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Why withdrawest Thou Thy hand, even Thy right hand? Draw it out of Thy bosom and consume them.
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Yet God is my King of old, working salvation in the midst of the earth.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Thou didst break the sea in pieces by Thy strength; Thou didst shatter the heads of the sea-monsters in the waters.
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Thou didst crush the heads of leviathan, Thou gavest him to be food to the folk inhabiting the wilderness.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Thou didst cleave fountain and brook; Thou driedst up ever-flowing rivers.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Thine is the day, Thine also the night; Thou hast established luminary and sun.
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Thou hast set all the borders of the earth; Thou hast made summer and winter.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Remember this, how the enemy hath reproached the LORD, and how a base people have blasphemed Thy name.
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 O deliver not the soul of Thy turtle-dove unto the wild beast; forget not the life of Thy poor for ever.
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Look upon the covenant; for the dark places of the land are full of the habitations of violence.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 O let not the oppressed turn back in confusion; let the poor and needy praise Thy name.
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Arise, O God, plead Thine own cause; remember Thy reproach all the day at the hand of the base man.
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Forget not the voice of Thine adversaries, the tumult of those that rise up against Thee which ascendeth continually.
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

< Psalms 74 >