< Psalms 72 >

1 A Psalm of Solomon. Give the king Thy judgments, O God, and Thy righteousness unto the king's son;
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 That he may judge Thy people with righteousness, and Thy poor with justice.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Let the mountains bear peace to the people, and the hills, through righteousness.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 May he judge the poor of the people, and save the children of the needy, and crush the oppressor.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 They shall fear Thee while the sun endureth, and so long as the moon, throughout all generations.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 May he come down like rain upon the mown grass, as showers that water the earth.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 In his days let the righteous flourish, and abundance of peace, till the moon be no more.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 May he have dominion also from sea to sea, and from the River unto the ends of the earth.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Let them that dwell in the wilderness bow before him; and his enemies lick the dust.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 The kings of Tarshish and of the isles shall render tribute; the kings of Sheba and Seba shall offer gifts.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Yea, all kings shall prostrate themselves before him; all nations shall serve him.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 For he will deliver the needy when he crieth; the poor also, and him that hath no helper.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 He will have pity on the poor and needy, and the souls of the needy he will save.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 He will redeem their soul from oppression and violence, and precious will their blood be in his sight;
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 That they may live, and that he may give them of the gold of Sheba, that they may pray for him continually, yea, bless him all the day.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 May he be as a rich cornfield in the land upon the top of the mountains; may his fruit rustle like Lebanon; and may they blossom out of the city like grass of the earth.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 May his name endure for ever; may his name be continued as long as the sun; may men also bless themselves by him; may all nations call him happy.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Blessed be the LORD God, the God of Israel, who only doeth wondrous things;
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 And blessed be His glorious name for ever; and let the whole earth be filled with His glory. Amen, and Amen.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 The prayers of David the son of Jesse are ended.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Psalms 72 >