< Psalms 63 >
1 A Psalm of David, when he was in the wilderness of Judah. O God, Thou art my God, earnestly will I seek Thee; my soul thirsteth for Thee, my flesh longeth for Thee, in a dry and weary land, where no water is.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 So have I looked for Thee in the sanctuary, to see Thy power and Thy glory.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 For Thy lovingkindness is better than life; my lips shall praise Thee.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 So will I bless Thee as long as I live; in Thy name will I lift up my hands.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 My soul is satisfied as with marrow and fatness; and my mouth doth praise Thee with joyful lips;
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 When I remember Thee upon my couch, and meditate on Thee in the night-watches.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 For Thou hast been my help, and in the shadow of Thy wings do I rejoice.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 My soul cleaveth unto Thee; Thy right hand holdeth me fast.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 But those that seek my soul, to destroy it, shall go into the nethermost parts of the earth.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 They shall be hurled to the power of the sword; they shall be a portion for foxes.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the king shall rejoice in God; every one that sweareth by Him shall glory; for the mouth of them that speak lies shall be stopped.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.