< Psalms 6 >

1 For the Leader; with string-music; on the Sheminith. A Psalm of David. O LORD, rebuke me not in Thine anger, neither chasten me in Thy wrath.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Be gracious unto me, O LORD, for I languish away; heal me, O LORD, for my bones are affrighted.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 My soul also is sore affrighted; and Thou, O LORD, how long?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Return, O LORD, deliver my soul; save me for Thy mercy's sake.
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For in death there is no remembrance of Thee; in the nether-world who will give Thee thanks? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 I am weary with my groaning; every night make I my bed to swim; I melt away my couch with my tears.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Mine eye is dimmed because of vexation; it waxeth old because of all mine adversaries.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Depart from me, all ye workers of iniquity; for the LORD hath heard the voice of my weeping.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 The LORD hath heard my supplication; the LORD receiveth my prayer.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 All mine enemies shall be ashamed and sore affrighted; they shall turn back, they shall be ashamed suddenly.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalms 6 >