< Psalms 47 >

1 For the Leader; a Psalm for the sons of Korah. O clap your hands, all ye peoples; shout unto God with the voice of triumph.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 For the LORD is most high, awful; a great King over all the earth.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 He subdueth peoples under us, and nations under our feet.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 He chooseth our inheritance for us, the pride of Jacob whom He loveth. (Selah)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 God is gone up amidst shouting, the LORD amidst the sound of the horn.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Sing praises to God, sing praises; sing praises unto our King, sing praises.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 For God is the King of all the earth; sing ye praises in a skilful song.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 God reigneth over the nations; God sitteth upon His holy throne.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 The princes of the peoples are gathered together, the people of the God of Abraham; for unto God belong the shields of the earth; He is greatly exalted.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Psalms 47 >