< Psalms 34 >
1 A Psalm of David; when he changed his demeanour before Abimelech, who drove him away, and he departed. I will bless the LORD at all times; His praise shall continually be in my mouth.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 My soul shall glory in the LORD; the humble shall hear thereof, and be glad.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 O magnify the LORD with me, and let us exalt His name together.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 I sought the LORD, and He answered me, and delivered me from all my fears.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 They looked unto Him, and were radiant; and their faces shall never be abashed.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 This poor man cried, and the LORD heard, and saved him out of all his troubles.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 The angel of the LORD encampeth round about them that fear Him, and delivereth them.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 O consider and see that the LORD is good; happy is the man that taketh refuge in Him.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 O fear the LORD, ye His holy ones; for there is no want to them that fear Him.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 The young lions do lack, and suffer hunger; but they that seek the LORD want not any good thing.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Come, ye children, hearken unto me; I will teach you the fear of the LORD.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Who is the man that desireth life, and loveth days, that he may see good therein?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Keep thy tongue from evil, and thy lips from speaking guile.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Depart from evil, and do good; seek peace, and pursue it.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 The eyes of the LORD are toward the righteous, and His ears are open unto their cry.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 The face of the LORD is against them that do evil, to cut off the remembrance of them from the earth.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 They cried, and the LORD heard, and delivered them out of all their troubles.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 The LORD is nigh unto them that are of a broken heart, and saveth such as are of a contrite spirit.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Many are the ills of the righteous, but the LORD delivereth him out of them all.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 He keepeth all his bones; not one of them is broken.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Evil shall kill the wicked; and they that hate the righteous shall be held guilty.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 The LORD redeemeth the soul of His servants; and none of them that take refuge in Him shall be desolate.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.