< Psalms 31 >

1 For the Leader. A Psalm of David. In thee, O LORD, have I taken refuge; let me never be ashamed; deliver me in Thy righteousness.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Incline Thine ear unto me, deliver me speedily; be Thou to me a rock of refuge, even a fortress of defence, to save me.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 For Thou art my rock and my fortress; therefore for Thy name's sake lead me and guide me.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Bring me forth out of the net that they have hidden for me; for Thou art my stronghold.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Into Thy hand I commit my spirit; Thou hast redeemed me, O LORD, Thou God of truth.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 I hate them that regard lying vanities; but I trust in the LORD.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 I will be glad and rejoice in Thy lovingkindness; for Thou hast seen mine affliction, Thou hast taken cognizance of the troubles of my soul,
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 And Thou hast not given me over into the hand of the enemy; Thou hast set my feet in a broad place.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Be gracious unto me, O LORD, for I am in distress; mine eye wasteth away with vexation, yea, my soul and my body.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 For my life is spent in sorrow, and my years in sighing; my strength faileth because of mine iniquity, and my bones are wasted away.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Because of all mine adversaries I am become a reproach, yea, unto my neighbours exceedingly, and a dread to mine acquaintance; they that see me without flee from me.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 I am forgotten as a dead man out of mind; I am like a useless vessel.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 For I have heard the whispering of many, terror on every side; while they took counsel together against me, they devised to take away my life.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 But as for me, I have trusted in Thee, O LORD; I have said: 'Thou art my God.'
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 My times are in Thy hand; deliver me from the hand of mine enemies, and from them that persecute me.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Make Thy face to shine upon Thy servant; save me in Thy lovingkindness.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 O LORD, let me not be ashamed, for I have called upon Thee; let the wicked be ashamed, let them be put to silence in the nether-world. (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 Let the lying lips be dumb, which speak arrogantly against the righteous, with pride and contempt.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Oh how abundant is Thy goodness, which Thou hast laid up for them that fear Thee; which Thou hast wrought for them that take their refuge in Thee, in the sight of the sons of men!
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Thou hidest them in the covert of Thy presence from the plottings of man; Thou concealest them in a pavilion from the strife of tongues.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Blessed be the LORD; for He hath shown me His wondrous lovingkindness in an entrenched city.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 As for me, I said in my haste: 'I am cut off from before Thine eyes'; nevertheless Thou heardest the voice of my supplications when I cried unto Thee.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 O love the LORD, all ye His godly ones; the LORD preserveth the faithful, and plentifully repayeth him that acteth haughtily.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Be strong, and let your heart take courage, all ye that wait for the LORD.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Psalms 31 >