< Psalms 18 >

1 For the Leader. A Psalm of David the servant of the LORD, who spoke unto the LORD the words of this song in the day that the LORD delivered him from the hand of all his enemies, and from the hand of Saul; And he said: I love thee, O LORD, my strength.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 The LORD is my rock, and my fortress, and my deliverer; my God, my rock, in Him I take refuge; my shield, and my horn of salvation, my high tower.
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 Praised, I cry, is the LORD, and I am saved from mine enemies.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 The cords of Death compassed me, and the floods of Belial assailed me.
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 The cords of Sheol surrounded me; the snares of Death confronted me. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
6 In my distress I called upon the LORD, and cried unto my God; out of His temple He heard my voice, and my cry came before Him unto His ears.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 Then the earth did shake and quake, the foundations also of the mountains did tremble; they were shaken, because He was wroth.
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 Smoke arose up in His nostrils, and fire out of His mouth did devour; coals flamed forth from Him.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 He bowed the heavens also, and came down; and thick darkness was under His feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 And He rode upon a cherub, and did fly; yea, He did swoop down upon the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 He made darkness His hiding-place, His pavilion round about Him; darkness of waters, thick clouds of the skies.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 At the brightness before Him, there passed through His thick clouds hailstones and coals of fire.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 The LORD also thundered in the heavens, and the Most High gave forth His voice; hailstones and coals of fire.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 And He sent out His arrows, and scattered them; and He shot forth lightnings, and discomfited them.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 And the channels of waters appeared, and the foundations of the world were laid bare, at Thy rebuke, O LORD, at the blast of the breath of Thy nostrils.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 He sent from on high, He took me; He drew me out of many waters.
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 He delivered me from mine enemy most strong, and from them that hated me, for they were too mighty for me.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 They confronted me in the day of my calamity; but the LORD was a stay unto me.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 He brought me forth also into a large place; He delivered me, because He delighted in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 The LORD rewarded me according to my righteousness; according to the cleanness of my hands hath He recompensed me.
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 For I have kept the ways of the LORD, and have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 For all His ordinances were before me, and I put not away His statutes from me.
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 And I was single-hearted with Him, and I kept myself from mine iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 Therefore hath the LORD recompensed me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in His eyes.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 With the merciful Thou dost show Thyself merciful, with the upright man Thou dost show Thyself upright;
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 With the pure Thou dost show Thyself pure; and with the crooked Thou dost show Thyself subtle.
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 For Thou dost save the afflicted people; but the haughty eyes Thou dost humble.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 For Thou dost light my lamp; the LORD my God doth lighten my darkness.
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 For by Thee I run upon a troop; and by my God do I scale a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 As for God, His way is perfect; the word of the LORD is tried; He is a shield unto all them that take refuge in Him.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 For who is God, save the LORD? And who is a Rock, except our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 The God that girdeth me with strength, and maketh my way straight;
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 Who maketh my feet like hinds', and setteth me upon my high places;
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 Who traineth my hands for war, so that mine arms do bend a bow of brass.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 Thou hast also given me Thy shield of salvation, and Thy right hand hath holden me up; and Thy condescension hath made me great.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 Thou hast enlarged my steps under me, and my feet have not slipped.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 I have pursued mine enemies, and overtaken them; neither did I turn back till they were consumed.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 I have smitten them through, so that they are not able to rise; they are fallen under my feet.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 For Thou hast girded me with strength unto the battle; Thou hast subdued under me those that rose up against me.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 Thou hast also made mine enemies turn their backs unto me, and I did cut off them that hate me.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 They cried, but there was none to save; even unto the LORD, but He answered them not.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 Then did I beat them small as the dust before the wind; I did cast them out as the mire of the streets.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 Thou hast delivered me from the contentions of the people; Thou hast made me the head of the nations; a people whom I have not known serve me.
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 As soon as they hear of me, they obey me; the sons of the stranger dwindle away before me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 The sons of the stranger fade away, and come trembling out of their close places.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 The LORD liveth, and blessed be my Rock; and exalted be the God of my salvation;
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 Even the God that executeth vengeance for me, and subdueth peoples under me.
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 He delivereth me from mine enemies; yea, Thou liftest me up above them that rise up against me; Thou deliverest me from the violent man.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 Therefore I will give thanks unto Thee, O LORD, among the nations, and will sing praises unto Thy name.
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 Great salvation giveth He to His king; and showeth mercy to His anointed, to David and to his seed, for evermore.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

< Psalms 18 >