< Psalms 138 >
1 A Psalm of David. I will give Thee thanks with my whole heart, in the presence of the mighty will I sing praises unto Thee.
Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 I will bow down toward Thy holy temple, and give thanks unto Thy name for Thy mercy and for Thy truth; for Thou hast magnified Thy word above all Thy name.
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
3 In the day that I called, Thou didst answer me; Thou didst encourage me in my soul with strength.
Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 All the kings of the earth shall give Thee thanks, O LORD, for they have heard the words of Thy mouth.
Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 Yea, they shall sing of the ways of the LORD; for great is the glory of the LORD.
Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 For though the LORD be high, yet regardeth He the lowly, and the haughty He knoweth from afar.
Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Though I walk in the midst of trouble, Thou quickenest me; Thou stretchest forth Thy hand against the wrath of mine enemies, and Thy right hand doth save me.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 The LORD will accomplish that which concerneth me; Thy mercy, O LORD, endureth for ever; forsake not the work of Thine own hands.
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.