< Psalms 137 >

1 By the rivers of Babylon, there we sat down, yea, we wept, when we remembered Zion.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Upon the willows in the midst thereof we hanged up our harps.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 For there they that led us captive asked of us words of song, and our tormentors asked of us mirth: 'Sing us one of the songs of Zion.'
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 How shall we sing the LORD'S song in a foreign land?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 If I forget thee, O Jerusalem, let my right hand forget her cunning.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Let my tongue cleave to the roof of my mouth, if I remember thee not; if I set not Jerusalem above my chiefest joy.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Remember, O LORD, against the children of Edom the day of Jerusalem; who said: 'Rase it, rase it, even to the foundation thereof.'
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 O daughter of Babylon, that art to be destroyed; happy shall he be, that repayeth thee as thou hast served us.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Happy shall he be, that taketh and dasheth thy little ones against the rock.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psalms 137 >