< Psalms 13 >

1 For the Leader. A Psalm of David. How long, O LORD, wilt Thou forget me for ever? How long wilt Thou hide Thy face from me?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 How long shall I take counsel in my soul, having sorrow in my heart by day? How long shall mine enemy be exalted over me?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Behold Thou, and answer me, O LORD my God; lighten mine eyes, lest I sleep the sleep of death;
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 Lest mine enemy say: 'I have prevailed against him'; lest mine adversaries rejoice when I am moved.
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 But as for me, in Thy mercy do I trust; my heart shall rejoice in Thy salvation.
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 I will sing unto the LORD, because He hath dealt bountifully with me.
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.

< Psalms 13 >