< Psalms 116 >
1 I love that the LORD should hear my voice and my supplications.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Because He hath inclined His ear unto me, therefore will I call upon Him all my days.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 The cords of death compassed me, and the straits of the nether-world got hold upon me; I found trouble and sorrow. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 But I called upon the name of the LORD: 'I beseech thee, O LORD, deliver my soul.'
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Gracious is the LORD, and righteous; yea, our God is compassionate.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 The LORD preserveth the simple; I was brought low, and He saved me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Return, O my soul, unto Thy rest; for the LORD hath dealt bountifully with thee.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For thou hast delivered my soul from death, mine eyes from tears, and my feet from stumbling.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I shall walk before the LORD in the lands of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I trusted even when I spoke: 'I am greatly afflicted.'
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I said in my haste: 'All men are liars.'
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 How can I repay unto the LORD all His bountiful dealings toward me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will lift up the cup of salvation, and call upon the name of the LORD.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 My vows will I pay unto the LORD, yea, in the presence of all His people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the sight of the LORD is the death of His saints.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 I beseech Thee, O LORD, for I am Thy servant; I am Thy servant, the son of Thy handmaid; Thou hast loosed my bands.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will offer to thee the sacrifice of thanksgiving, and will call upon the name of the LORD.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will pay my vows unto the LORD, yea, in the presence of all His people;
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 In the courts of the LORD'S house, in the midst of thee, O Jerusalem. Hallelujah.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.