< Psalms 114 >
1 When Israel came forth out of Egypt, the house of Jacob from a people of strange language;
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judah became His sanctuary, Israel His dominion.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The sea saw it, and fled; the Jordan turned backward.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 The mountains skipped like rams, the hills like young sheep.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 What aileth thee, O thou sea, that thou fleest? thou Jordan, that thou turnest backward?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ye mountains, that ye skip like rams; ye hills, like young sheep?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Tremble, thou earth, at the presence of the Lord, at the presence of the God of Jacob;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Who turned the rock into a pool of water, the flint into a fountain of waters.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.