< Psalms 105 >

1 O give thanks unto the LORD, call upon His name; make known His doings among the peoples.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Sing unto Him, sing praises unto Him; speak ye of all His marvellous works.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Glory ye in His holy name; let the heart of them rejoice that seek the LORD.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Seek ye the LORD and His strength; seek His face continually.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Remember His marvellous works that He hath done, His wonders, and the judgments of His mouth;
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 O ye seed of Abraham His servant, ye children of Jacob, His chosen ones.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 He is the LORD our God; His judgments are in all the earth.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 He hath remembered His covenant for ever, the word which He commanded to a thousand generations;
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 The covenant which He made with Abraham, and His oath unto Isaac;
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 And He established it unto Jacob for a statute, to Israel for an everlasting covenant;
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Saying: 'Unto thee will I give the land of Canaan, the lot of your inheritance.'
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 When they were but a few men in number. Yea, very few, and sojourners in it,
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 And when they went about from nation to nation, from one kingdom to another people,
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 He suffered no man to do them wrong, yea, for their sake He reproved kings:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 'Touch not Mine anointed ones, and do My prophets no harm.'
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 And He called a famine upon the land; He broke the whole staff of bread.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 He sent a man before them; Joseph was sold for a servant;
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 His feet they hurt with fetters, his person was laid in iron;
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Until the time that his word came to pass, the word of the LORD tested him.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 The king sent and loosed him; even the ruler of the peoples, and set him free.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 He made him lord of his house, and ruler of all his possessions;
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 To bind his princes at his pleasure, and teach his elders wisdom.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Israel also came into Egypt; and Jacob sojourned in the land of Ham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 And He increased His people greatly, and made them too mighty for their adversaries.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 He turned their heart to hate His people, to deal craftily with His servants.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 He sent Moses His servant, and Aaron whom He had chosen.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 They wrought among them His manifold signs, and wonders in the land of Ham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 He sent darkness, and it was dark; and they rebelled not against His word.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 He turned their waters into blood, and slew their fish.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Their land swarmed with frogs, in the chambers of their kings.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 He spoke, and there came swarms of flies, and gnats in all their borders.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 He gave them hail for rain, and flaming fire in their land.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 He smote their vines also and their fig-trees; and broke the trees of their borders.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 He spoke, and the locust came, and the canker-worm without number,
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 And did eat up every herb in their land, and did eat up the fruit of their ground.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 He smote also all the first-born in their land, the first-fruits of all their strength.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 And He brought them forth with silver and gold; and there was none that stumbled among His tribes.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Egypt was glad when they departed; for the fear of them had fallen upon them.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 He spread a cloud for a screen; and fire to give light in the night.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 They asked, and He brought quails, and gave them in plenty the bread of heaven.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 He opened the rock, and waters gushed out; they ran, a river in the dry places.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 For He remembered His holy word unto Abraham His servant;
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 And He brought forth His people with joy, His chosen ones with singing.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 And He gave them the lands of the nations, and they took the labour of the peoples in possession;
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 That they might keep His statutes, and observe His laws. Hallelujah.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 105 >