< Proverbs 1 >

1 THE PROVERBS of Solomon the son of David, king of Israel;
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 To know wisdom and instruction; to comprehend the words of understanding;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 To receive the discipline of wisdom, justice, and right, and equity;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 To give prudence to the simple, to the young man knowledge and discretion;
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 That the wise man may hear, and increase in learning, and the man of understanding may attain unto wise counsels;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 To understand a proverb, and a figure; the words of the wise, and their dark sayings.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 The fear of the LORD is the beginning of knowledge; but the foolish despise wisdom and discipline.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Hear, my son, the instruction of thy father, and forsake not the teaching of thy mother;
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 For they shall be a chaplet of grace unto thy head, and chains about thy neck.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 My son, if sinners entice thee, consent thou not.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 If they say: 'Come with us, let us lie in wait for blood, let us lurk for the innocent without cause;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Let us swallow them up alive as the grave, and whole, as those that go down into the pit; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 We shall find all precious substance, we shall fill our houses with spoil;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Cast in thy lot among us; let us all have one purse' —
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 My son, walk not thou in the way with them, restrain thy foot from their path;
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 For their feet run to evil, and they make haste to shed blood.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 For in vain the net is spread in the eyes of any bird;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 And these lie in wait for their own blood, they lurk for their own lives.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 So are the ways of every one that is greedy of gain; it taketh away the life of the owners thereof.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Wisdom crieth aloud in the streets, she uttereth her voice in the broad places;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 She calleth at the head of the noisy streets, at the entrances of the gates, in the city, she uttereth her words:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 'How long, ye thoughtless, will ye love thoughtlessness? And how long will scorners delight them in scorning, and fools hate knowledge?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Turn you at my reproof; behold, I will pour out my spirit unto you, I will make known my words unto you.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Because I have called, and ye refused, I have stretched out my hand, and no man attended,
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 But ye have set at nought all my counsel, and would none of my reproof;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 I also, in your calamity, will laugh, I will mock when your dread cometh;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 When your dread cometh as a storm, and your calamity cometh on as a whirlwind; when trouble and distress come upon you.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Then will they call me, but I will not answer, they will seek me earnestly, but they shall not find me.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 For that they hated knowledge, and did not choose the fear of the LORD;
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 They would none of my counsel, they despised all my reproof.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Therefore shall they eat of the fruit of their own way, and be filled with their own devices.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 For the waywardness of the thoughtless shall slay them, and the confidence of fools shall destroy them.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 But whoso hearkeneth unto me shall dwell securely, and shall be quiet without fear of evil.'
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbs 1 >