< Proverbs 8 >

1 Doth not wisdom call, and understanding put forth her voice?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 In the top of high places by the way, where the paths meet, she standeth;
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Beside the gates, at the entry of the city, at the coming in at the doors, she crieth aloud:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 'Unto you, O men, I call, and my voice is to the sons of men.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 O ye thoughtless, understand prudence, and, ye fools, be ye of an understanding heart.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Hear, for I will speak excellent things, and the opening of my lips shall be right things.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 For my mouth shall utter truth, and wickedness is an abomination to my lips.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 All the words of my mouth are in righteousness, there is nothing perverse or crooked in them.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 They are all plain to him that understandeth, and right to them that find knowledge.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Receive my instruction, and not silver, and knowledge rather than choice gold.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 For wisdom is better than rubies, and all things desirable are not to be compared unto her.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 I wisdom dwell with prudence, and find out knowledge of devices.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 The fear of the LORD is to hate evil; pride, and arrogancy, and the evil way, and the froward mouth, do I hate.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Counsel is mine, and sound wisdom; I am understanding, power is mine.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 By me kings reign, and princes decree justice.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 By me princes rule, and nobles, even all the judges of the earth.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 I love them that love me, and those that seek me earnestly shall find me.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Riches and honour are with me; yea, enduring riches and righteousness.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 My fruit is better than gold, yea, than fine gold; and my produce than choice silver.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 I walk in the way of righteousness, in the midst of the paths of justice;
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 That I may cause those that love me to inherit substance, and that I may fill their treasuries.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 The LORD made me as the beginning of His way, the first of His works of old.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 I was set up from everlasting, from the beginning, or ever the earth was.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 When there were no depths, I was brought forth; when there were no fountains abounding with water.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Before the mountains were settled, before the hills was I brought forth;
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 While as yet He had not made the earth, nor the fields, nor the beginning of the dust of the world.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 When He established the heavens, I was there; when He set a circle upon the face of the deep,
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 When He made firm the skies above, when the fountains of the deep showed their might,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 When He gave to the sea His decree, that the waters should not transgress His commandment, when He appointed the foundations of the earth;
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Then I was by Him, as a nursling; and I was daily all delight, playing always before Him,
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Playing in His habitable earth, and my delights are with the sons of men.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Now therefore, ye children, hearken unto me; for happy are they that keep my ways.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Hear instruction, and be wise, and refuse it not.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Happy is the man that hearkeneth to me, watching daily at my gates, waiting at the posts of my doors.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 For whoso findeth me findeth life, and obtaineth favour of the LORD.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 But he that misseth me wrongeth his own soul; all they that hate me love death.'
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Proverbs 8 >